MTENDERE
Munali mtendere mu Lusaka
yitatha miyezi inai ya
kumenya mvula yaukali.
Namondwe anapopoma
po po po.
Zigumula zidalephera
kugonjetsa Mzinda wathu.
Lusaka yinamenya
kusintha kwanyengo.
PEACE
There was peace in Lusaka
after four months of
fighting furious rains.
The deluge wooshed
woosh woosh woosh.
Floods had failed
to defeat our city.
Lusaka fought
climate change.
KUFUNDA KWADZIKO
Lusaka yikuŵefemuka
befu befu befu.
Kufunda kwadziko kwabweretsa
kutentha nyengo yozizira iyi. Modabwitsa,
Mzinda wathu uli wotentha
m’mwezi wa Cisanu.
Zotuluka zingakhale cifukwa.
Lero limveka monga
masana a Mafundi.
GLOBAL WARMING
Lusaka is panting
pant pant pant.
Global warming has brought
heat this cold season.
Surprisingly,
our City is hot
in the month of June.
Emissions could be the reason.
Today feels like
an October afternoon.
MKHALIDWE
Moto winanso ukubuka
bhu bhu bhu.
Mkhalidwe umakhala uipitsidwa
monga mtima wacinyengo
ngati anthu aotcha zinyalala.
Dera lathu lipuma mphepo yauve
pamene malaŵi apsereza zapadzala.
Zoipitsa izi
zili bvuto lopanga munthu
zimene zisautsa Dziko Lapansi.
Winawake anali kuotcha zinyatsi
m’bwalo usiku watha.
Utsi wonyansa ukuipitsa
mkhalidwe wathu.
THE ENVIRONMENT
Another fire is crackling
crackle crackle crackle.
The environment becomes polluted
like a corrupt heart
when people burn rubbish.
Our community breathes dirty air
as flames incinerate garbage.
This pollution
is a man-made problem
that pesters Planet Earth.
Someone was burning trash
in a yard last night.
Filthy smoke is polluting
our environment.
MAZIKO
Nsanja Bennie Mwiinga ndi
cimango cacitali
m’mtima wodukhula
wa dera lathu
du du du.
Nsonga yikukhudza mlengalenga.
Ndi copangidwa ca citsulo.
Nsanja, yopakidwa
cofiira ndi coyera,
ifika mitambo.
Monga zolukanalukana
zikuteteza mitima yathu,
mpanda uzinga maziko
pa Mseu Bennie Mwiinga.
THE BASE
Bennie Mwiinga Tower is
the tallest structure
in the throbbing heart
of our community
throb throb throb.
The tip touches the sky.
It is made of iron.
The Tower, painted
red and white,
reaches clouds.
Like networks
safeguarding our hearts,
a fence surrounds the base
on Bennie Mwiinga Road.
WOKALAMBA
Ankhanza aŵiri akankha citseko cimene
mkazi wokalamba akukankhaso.
Iye ayesa kugwira
tabwa monga cishango.
Nkhanza yao ilandira kutchingira.
Mphamvu yake ivumbulika
kwa alionse amene achepetsa
kupitirizika kwa ukalamba.
Iye atchinga nkhanza
pakukana kukhala osoŵa.
Wankhanza yense akukankha
mwacigogogo, koma wokalamba wathu
wakhoza kupotokola cifungulo koo.
ELDER
Two abusers push a door that
an elderly woman is pushing back.
She tries to wield
the wood like a shield.
Their abuse receives resistance.
Her power is revealed
to anybody who underrates
the persistence of old age.
She resists abuse
by refusing to be disadvantaged.
Each abuser is pushing
forcefully, but our elder
has managed to twist a key.
KUPIKISANA
Ana atatu anali kuthamanga
pamwamba ndi pansi pamakwerera
m’cimangidwe citali
pafupi ndi Citunda ca Manda.
Atauluka zosanja zisanu,
iwo anapikisana kunsanjika kunsi.
Othamanga anali ndi
zikonzeko zaseŵero.
Wothamanga wacimodzi
anadutsadutsa makwerera,
koma iye sanapate.
Wina waciŵiri analumpha
kwerera kena konse
ndipo nalephera.
Mwana wacitatu anapata mpikisano
pakuthamanga m’cingwe coongoka.
RACING
Three children were running
up and down the stairs
in a tall building
near Manda Hill.
After soaring five storeys,
they raced to the ground floor.
The runners had
game plans.
The first runner
crisscrossed the stairs,
but he did not win.
The second one jumped
every other stair
and lost.
The third child won the race
by running in a straight line.
MLATHO
Kakongoledwe ka Mlatho Munali
ndi kosatsutsika. Cing’anima usiku.
Ise tilibe kanthu kokanganapo.
Mlatho uthetsa mabvuto amseu.
Palibe cotsutsa.
Kukoma kwa Mlatho wa Munali
sikunakanganepo. Cinyezimira
pa Mseu Waukulu Wakum’maŵa.
Mlatho Munali uimilira mokongola.
BRIDGE
The magnificence of Munali Bridge
is undeniable. It sparkles at night.
We have nothing to debate.
The Bridge solves road problems.
There is no denying.
The beauty of Munali’s Bridge
has never been debatable. It glitters
on Great East Road.
Munali Bridge stands magnificently.
VWENDE
Ine ndinagula vwende yaing’ono
pa Msika Mtendere pafupi ndi kwathu.
Mitengo yinandipangitsa kufoka.
M’mero wanga unatsamwitsa
pa cizizwitso cowawa.
Zikulu zinali makwacha makumi asanu
ngati kuti mtengo udonsa msampha.
Zipatso zakhala zodula cwii
ngakhale kuti kunzuna
kulibe phindu lero.
Vwende yotsika yinali
makwacha makumi aŵiri mlungu watha.
M’kuthenta kwa nyumba,
banja langa linayidya lonyowa
monga mikango yikukukuta mbeŵa.
Cipatso cinanunkhira kufiira mkati fii.
WATERMELON
I bought a small watermelon
at Mtendere Market near home.
The prices made me weak.
My throat choked
on bitter astonishment.
Big ones were fifty kwacha
as if the price pulled a prank.
Fruits have become expensive
even though sweetness
has no value today.
The cheapest watermelon was
twenty kwacha last week.
In the heat of the house,
my family ate it wet
like lions gnashing a mouse.
The fruit smelled red inside.
MWAZI
Kusonkha mwazi kugalamutsa
mantha acibadwa.
Ise tikusisima ngati
madontho ofiira ati tho tho tho.
Kuopa kuŵaŵa
ndi udani wa nsingano
zilepheretsa anthu amantha.
Opeŵa akumatakataka
ndi kunjenjema
pamene ziphuphu ziuma.
Izi zoopa zionetsa kuti
msonkho wamwazi
uli nsembe yakudzimana.
Osonkha mwazi ali ndi
olimba mtima kupirira
kamphindi kamodzi koŵaŵa.
BLOOD
Donating blood arouses
natural terror.
We are whimpering when
red drops drip drip drip.
Fear of pain
and hatred of needles
deter terrified people.
Abstainers are squirming
and shivering
as goosebumps stiffen.
These fears suggest that
blood donation
is a selfless sacrifice.
The blood donors have
the strength of heart to endure
one painful moment.
KHUNGU
Mwamuna mwabi akufotokoza kuti
cimaphatikizapo citha
kunyoza kwakhungu.
Ubwenzi umveka monga linga
lokana cisokonezo kapena kusungulumwa
pamene amfunzi ayesa kukhetsa
ulemu ndi cigamulo cake.
Cipinda ciuka ndi kuomba
kwa kwa kwa.
Abwenzi ayenera kuthandiza
ngati akakumane ndi tsankho. M’cipanduko caphatikiziramo,
anzanu angathetse kupatulana.
SKIN
An albino man is explaining that
inclusion combats
skin shaming.
Friendship feels like a fortress
against confusion or alienation
when bullies try draining
his dignity and determination.
The room rises to applaud
clap clap clap.
Friends must help
if he faces discrimination.
In an inclusive revolution,
allies can invalidate exclusion.
MTSINJE WA ZAMBEZI
Madzi akhala akuŵira
kucokera nthawi
Dziko Lapansi linalengedwa
kubwi-kubwi kubwi-kubwi.
Tsopano pano,
Mtsinje wa Zambezi ukuyenda
kumalo aakulu a madzi.
Iye ali mulendo wakukuŵirira koposa.
Kucokera gwero mu Mwinilunga,
mfuleni udzakapita
kumkhate wokulirapo kumene
pfunde lililonse lidzafutukula ndi kuchepa.
Monga mai wolemekezeka,
Zambezi yimapereka
moyo kucigaŵo cokhutira.
Mkaka wake umaukitsa aliyense.
Mitsinje ya Zambia
yimayenda padziko lonse.
ZAMBEZI RIVER
Water has been babbling
from the time
Planet Earth was formed
babble babble babble.
Right now,
the Zambezi River is flowing
to a bigger body of water.
She is the bubbliest traveller.
From the source in Mwinilunga,
the stream will be going
to a larger basin where
every tide will distend and subside.
Like a glorified mother,
the Zambezi does provide
life to a satisfied region.
Her milk revitalises everyone.
Zambia’s rivers
flow worldwide.
MSIRIRO
Cikondwerero cako
cinatiphunzitsa
kuti ndi codwalitsa
kusirira
khu khu khu.
Kususuka kuŵaŵa kwambiri
ayo mawe aa!
Msiriro ukulitsa nthenda
mmene kunyowa
kuoletsa mitengo.
Osusuka ayamba kudwala
ngati cisiriro ciumirira.
GREED
Your party
taught us
that it is sickening
to be greedy
glug glug glug.
Gluttony hurts so much
groan moan ouch!
Greed aggravates disease
the way sogginess
rots trees.
Gluttons start to be sick
when greediness persists.
NGODYA
Ngodya za kumpoto
zimathwanima masana onse
monga mitsempha ya leza
m’mitambo ya cikumbukiro.
Kuŵala kwadzuŵa kumaloŵa
mbali imodzi ya nyumba.
Kuunika kwakhala kutsetsereka
kodutsa mazenera kucokera m’maŵa.
Monga cikumbukiro ca cowawa,
ngodya yakumpoto ya
cipinda ciliconse yikuthwanima.
CORNERS
Corners in the north
flash all afternoon
like veins of lightning
in memory’s clouds.
Sunshine ingresses
one side of the house.
Light has been sliding
through windows from morning.
Like a memory of pain,
the northern corner of
each room is flashing.
AFRIKA
Afrika yili ndi msika umodzi.
Maiko makumi-asanu-mphambu-asanu
agulitsa mautumiki mu
Malo Amalonda Omasuka.
Colinga cathu ndi kuchirikiza
ufulu wacuma.
Zambia yimagula zipatso
kucokera EneAfrika popeza
mgwirizano uchirikiza cimasuko.
AFRICA
Africa has one market.
Fifty-five nations
sell services in the
Free Trade Area.
Our goal is to sustain
economic independence.
Zambia buys products
from Africans because
unity sustains freedom.
CILALA
Cilala cidaononga
zokolola, ndi cinabweretsa
njala monga munalibe mitengo
m’thengo cakaco.
Cinali ngati kuti mudzi
udali kudula nthambi
du du du.
Zilala zambiri zinadza.
THE DROUGHT
The drought had destroyed
crops, and it brought
hunger like there were no trees
in the forest that year.
It was as if the village
had been chopping branches
chop chop chop.
More droughts came.
WOPHUNZITSA WATHU
Wophunzitsa wathu amalemba maseŵero
omwe aposa kukanthidwa
kwa mphezi ya mphamvu ya magetsi.
Ise tili m’mdima, kupenyera
luntha la mwamunayo
pa ciunda cong’anima.
Zolemba zake zili zopambana
popeza iye ayanjanitsa
tsoka lokakala
ndi nthabwala zosalala.
Oseŵera aloŵeza mau ake
kuomvetsera omwe akulira
ndi kuseka tye tye tye.
Manja athu athokoza iyo
ndi bingu la citamando.
Mphunzitsi wanga
asonyeza kuti cikali cothekadi
kupambana monga wolemba-waseŵero.
OUR LECTURER
Our lecturer writes plays
that are more shocking
than a jolt of electric power.
We are in the dark, watching
the man’s imagination
on a sparkling stage.
His scripts are successful
since he juxtaposes
rough tragedy
and slick comedy.
Actors recite his words
to an audience that is crying
and laughing explosively.
Our hands thank him
with the thunder of acclaim.
My teacher
proves that it is still possible
to succeed as a playwright.
NDAKATULO
Tiyeni tikumane pa Nyanja za Goma.
Mudze ndi ndakatulo yanu.
Bweretsani malembo.
Amaluso adzakakumana
pa Maphunziro Apamwamba a Zambia.
Kodi nciani inu mukubweretsa?
Ine ndidzakadza ndi lembo langa.
Andakatulo akukumana za Nyanja.
POETRY
Let us meet at the Goma Lakes.
Come with your poetry.
Bring texts.
Artists will be meeting
at the University of Zambia.
What are you bringing?
I shall be coming with my text.
Poets are meeting by the Lakes.
KULEMA
Mtsikana adayasamula kuzindikiritsa kulema.
Iye anali kuyasamula
yasa yasa yasa.
Dzanja lofooka linabisa kamwa kotseguka.
Lidali tsiku lotopetsa.
Makolo ake anayamba kuyasamula nao.
“Ise ndise otopa,” iwo anena.
Banja linali kuyasamula mofuula.
Pakamwa pao panatseguka mokulitsidwa
monga mvuu zionetsa minyanga.
Mabanja ena anali kugona kale.
Maso a mtsikana anamveka olema,
koma iye anaphethira kuyang’ana kupyola.
“Ine ndine wotopa,” iye anayasamula.
FATIGUE
The girl had yawned to signify fatigue.
She was yawning
yawn yawn yawn.
A weak hand covered an open mouth.
It had been a tiring day.
Her parents began to yawn too.
“We are tired,” they said.
The family was yawning loudly.
Their mouths opened widely
like hippopotamuses exposing tusks.
Some families were sleeping already.
The girl’s eyes felt fatigued,
but she blinked to look beyond.
“I am tired,” she yawned.
GOMBE
Ngalaŵa paliŵiro lofanana
ndi ncenga yinanyamula
okwera kuoloka Nyanja Kariba, koma
iwo sanathe kutsika
popeza njobvu
khavaa khavaa pagombe.
SHORE
A boat speeding like
Brycinus lateralis carried passengers
across Lake Kariba, but
they could not disembark
because of elephants
splish-splashing on the shore.
KUTSATA
Ise tinatsata atsogoleri athu
monga ana akumverera kholo.
Ambiri adalondola
mphamvu ndi citsogozo mmene
tizilombo timakhamukira nyali.
Komabe, inu munali kulondola
utsogoleri ndi cidwi
ngati kudzimana kwa mtumiki.
Ine ndinali kutsata.
FOLLOWING
We followed our leaders
like children obeying a parent.
Many had pursued
power and influence the way
insects swarm lamps.
However, you were pursuing
leadership and impact
as selflessly as a servant.
I was following.
KUSITA
Ine ndinayesa kusita zovala
tacita zocapa, koma
kunalibe magetsi
m’nyumba usiku uja.
Zikonzeko zanga zinaoneka
ngati kuonongeka
kwa bowa wonyowa.
Zipinda zonse zinali mdima bii,
ndi citsulo cinali cozizira zii.
Magetsi sanabwerere, motero
ine ndinayenera kuvala
malaya amakwinya ngati
bowa wouma gwaa.
IRONING
I tried ironing clothes
after doing laundry, but
there was no electricity
in the house that night.
My plans seemed
as spoiled
as a soggy mushroom.
All rooms were dark,
and the iron was cold.
Electricity did not return, so
I had to wear
an outfit as wrinkled
as a dry mushroom.
MATUZA
Mulole cakudya cizizire zii.
Musapsetse lilimi lanu.
Kupupuluma kupanga matuza
omwe aphulika m’kamwa kanu
phu phu phu.
Yembekezani nthunzi licepe.
Cinali kuŵira mmphika,
motero cakudya ndi cotentha.
BLISTERS
Let the food cool.
Do not burn your tongue.
Rushing causes blisters
that burst in your mouth
pop pop pop.
Wait for the steam to subside.
It was boiling in the pot,
so the food is hot.
MFUMU
Mfumu ndi mutu wathu
mu Cumaconse ca Maiko.
Iye anali kalonga
mpaka mai wake anamwalira.
Ndodo anabweretsa kwa iyo.
Ngale zathu zaveka Mfumu.
THE KING
The King is our head
in the Commonwealth of Nations.
He was a prince
until his mother died.
The sceptre was brought to him.
Our jewels adorn the King.
CONDE
Conde kumbukirani
kukonzanso zinyalala
ndi kuzima nyali phii.
Kusintha kwanyengo
kwakhala kozunguza ngati
njoka yonyongana,
koma mayankho olama
adzabweza kufunda kwadziko.
PLEASE
Please remember
to recycle rubbish
and to turn off lights.
Climate change
has become as convoluted
as a twisted serpent,
but sensible solutions
will reverse global warming.
ALIONSE
Winawake adafesa mbeu
atagaula ponseponse
gau gau gau.
Kalikonse kangafale paja.
Mbeu ija inakula tsiku lililonse.
Alionse anatha kuona kuti
cinacake cinali kutuluka
kucokera m’nthaka yofeŵa.
Ndipo aliyense anayamba kufesa
mbeu yambiri pano.
ANYBODY
Someone had planted a seed
after digging everywhere
dig dig dig.
Anything can thrive there.
That seed grew every day.
Anybody could see that
something was emerging
from the soft soil.
Then everyone started to plant
more seeds here.
CISANGALALO
Cisangalalo cakhala cikucitika kwa ife.
Mitima yathu yikhetsa nthungululu
lu lu lu.
Cimveredwe cidzamariza, komabe
ise tikukonza tikhalebe osangalala.
Ntchito yingachirikize cimwemweci
ngati zikondwerero zatha.
Tiyeni tikonze kukhalabe osangalala.
Antchito alandira cidzikhutiro,
ndi okonza adzikondweretsa okha.
Cikondwero cingotuluka, koma
citenga khama kukondwera.
Cikonzeko canga cili kudzikhutiritsa
kotazimiririka mamveredwe aya.
Ine ndine wosangalala.
HAPPINESS
Happiness has been happening to us.
Our hearts ooze ululation
ululate ululate ululate.
The feeling will finish, however
we are planning to stay happy.
Work can sustain this bliss
when the celebrations cease.
Let us plan to remain happy.
Workers earn self-satisfaction,
and planners enjoy themselves.
Joy just emerges, but
it takes effort to rejoice.
My plan is to be self-satisfied
after these feelings fade.
I am happy.
MALIRE
Malire aoneketsa kudziŵika kwa Afrika.
Zingwe zadziko zitsimikiza udzilamuliro.
Kaonekedwe ka Zambia
ndi cithunzithunzi cokongola copangidwa ca malire ogwirizanitsana
a Zimbabwe kunsi kum’mwera,
Malaŵi ndi Mozambique
kulamanja kum’maŵa,
Congo kumwamba kumpoto, ndi
Angola kulamanzere kumadzulo.
Malire athu akugundana
gu gu gu.
Maiko a Afrika
agaŵana malire ogwirizana.
BORDERS
Borders shape Africa’s identity.
Country lines reinforce sovereignty.
The shape of Zambia
is a magnificent image made
by the unified borders
of Zimbabwe down south,
Malawi and Mozambique
to the right in the east,
The Congo up north, and
Angola to the left in the west.
Our borders are brushing
brush, brush, brush.
The nations of Africa
share united borders.
CINYANJADI
Indetu, ndi coona
kuti Cinyanja ndi cilankhulidwe cathu.
Mai wanga anabadwira mu Lusaka.
Inde, iye analoŵa miyambo yamadera.
Ana ake anabadwira mwa Kalingalinga.
Ndithu, Mzinda ulankhula kwa ife.
Coonadi ndi kuti tikhala mu Mtendere.
Indedi, Lusaka yikamba kwa ineyo.
Monga phokoso,
ine ndiyankha mu Cinyanjadi.
ACTUAL NYANJA
Absolutely, it is true
that Nyanja is our language.
My mother was born in Lusaka.
Yes, she inherited local traditions.
Her children were born in Kalingalinga.
Of course, the City speaks to us.
The truth is that we live in Mtendere.
Definitely, Lusaka talks to me.
Like an uproar,
I respond in actual Nyanja.
MATHITHI
Mlongo wao adapita yekha
kumathithi monga kakadzidzi
kauluka kokha
zee zee zee.
Iye anali kupita kodutsa nkhalango
pomwe mvula yitayamba kugwa
paka paka paka.
Monga akadzidzi asaka
nsomba kapena kalulu,
abale ake anapita
kumathithiwo,
koma iye sanaliko.
WATERFALL
Their sister had gone alone
to the waterfall like an owlet
soaring solo
soar soar soar.
She was going through the jungle
when rain started pouring
splish splish splish.
Like owls stalking
fish or hare,
her brothers went
to the same waterfall,
but she was not there.
CIUNDA
Akazi khumi adalankhula paciunda.
Ise tinaomba munsi mwa mitambo
monga zingiringiri m’kamvulumvulu.
Mphepo yinaloŵa mobangula;
tsindwi linali lotseguka.
Iwo adakhala akulankhula
kunsi kwa nyenyezi zophimba.
Mkazi wakhumi analankhula pansi
pamwezi wobisika. Anthu akhala
akuomba pamene iwo anasiya ciunda.
THE STAGE
Ten women had spoken on stage.
We clapped below clouds
like bells in whirlwinds.
Air entered with a roar;
the roof was open.
They had been speaking
beneath concealed stars.
The tenth woman spoke under
a hidden moon. People have been
clapping since they left the stage.